Salimo 123
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. 
 1 Ndikweza maso anga kwa Inu, 
kwa Inu amene mumakhala kumwamba. 
 2 Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo, 
monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake, 
choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu, 
mpaka atichitire chifundo. 
 3 Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo, 
pakuti tapirira chitonzo chachikulu. 
 4 Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza, 
chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.