Salimo 6
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. 
 1 Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, 
kapena kundilanga mu ukali wanu. 
 2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; 
Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu. 
 3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. 
Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti? 
 4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; 
pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika. 
 5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; 
Amakutamandani ndani ali ku manda? 
 6 Ine ndatopa ndi kubuwula; 
usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; 
ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi. 
 7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; 
akulephera kuona chifukwa cha adani anga. 
 8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, 
pakuti Yehova wamva kulira kwanga. 
 9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; 
Yehova walandira pemphero langa. 
 10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; 
adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.