49
Mtumiki wa Yehova 
 1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba 
tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: 
Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, 
ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga. 
 2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, 
anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; 
Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa 
ndipo anandibisa mʼchimake. 
 3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. 
Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.” 
 4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito 
ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, 
koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, 
ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.” 
 5 Yehova anandiwumba ine 
mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake 
kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye 
ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, 
choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, 
ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga. 
 6 Yehovayo tsono akuti, 
“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, 
kuti udzutse mafuko a Yakobo 
ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. 
Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, 
udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.” 
 7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, 
Woyerayo wa Israeli akunena, 
amene mitundu ya anthu inamuda, 
amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, 
“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. 
Akalonga nawonso adzagwada pansi. 
Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika 
ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.” 
Kubwezeretsedwa kwa Israeli 
 8 Yehova akuti, 
“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, 
ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; 
ndinakusunga ndi kukusandutsa 
kuti ukhale pangano kwa anthu, 
kuti dziko libwerere mwakale 
ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso. 
 9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke 
ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. 
“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira 
ndi msipu pa mʼmalo owuma. 
 10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, 
kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; 
chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera 
ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi. 
 11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, 
ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza. 
 12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, 
ena kumpoto, ena kumadzulo, 
enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.” 
 13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; 
kondwera, iwe dziko lapansi; 
imbani nyimbo inu mapiri! 
Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, 
ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika. 
 14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, 
Ambuye wandiyiwala.” 
 15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere 
ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? 
Ngakhale iye angathe kuyiwala, 
Ine sindidzakuyiwala iwe! 
 16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; 
makoma ako ndimawaona nthawi zonse. 
 17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, 
ndipo amene anakupasula akuchokapo. 
 18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane 
ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. 
Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, 
anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa 
chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’ 
 19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa 
ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, 
chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera 
ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali. 
 20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni 
adzanena kuti, 
‘Malo ano atichepera, 
tipatse malo ena woti tikhalemo.’ 
 21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, 
‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? 
Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; 
ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. 
Ndani anawalera ana amenewa? 
Ndinatsala ndekha, 
nanga awa, achokera kuti?’ ” 
 22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, 
“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. 
Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. 
Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo 
ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo. 
 23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera 
ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. 
Iwo adzagwetsa nkhope 
zawo pansi. 
Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; 
iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.” 
 24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, 
kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza? 
 25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, 
“Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, 
ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; 
ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, 
ndipo ndidzapulumutsa ana anu. 
 26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; 
adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. 
Zikadzatero anthu onse adzadziwa 
kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, 
Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”